Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 83:7-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Gebala ndi Amoni ndi Amaleki;Filistiya, pamodzi ndi iwo okhala m'Turo.

8. Asuri anaphatikana nao;Anakhala dzanja la ana a Loti,

9. Muwacitire monga munacitira Midyani;Ndi Sisera, ndi Jabini ku mtsinje wa Kisoni:

10. Amene anaonongeka ku Endoro;Anakhala ngati ndowe ya kumunda.

11. Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu;Mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna:

12. Amene anati, TilandeMalo okhalamo Mulungu, akhale athu.

13. Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;Ngati ziputu zomka ndi mphepo.

14. Monga moto upsereza nkhalango,Ndi monga lawi liyatsa mapiri;

15. Momwemo muwatsate ndi namondwe,Nimuwaopse ndi kabvumvulu wanu.

16. Acititseni manyazi pankhope pao;Kuti afune dzina lanu, Yehova.

17. Acite manyazi, naopsedwe kosatha;Ndipo asokonezeke, naonongeke:

18. Kuti adziwe kuti inu nokha, dzina lanu ndinu Yehova,Ndinu Wam'mwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 83