Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 83:6-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Mahema a Edomu ndi a Aismayeli;Moabu ndi Ahagara;

7. Gebala ndi Amoni ndi Amaleki;Filistiya, pamodzi ndi iwo okhala m'Turo.

8. Asuri anaphatikana nao;Anakhala dzanja la ana a Loti,

9. Muwacitire monga munacitira Midyani;Ndi Sisera, ndi Jabini ku mtsinje wa Kisoni:

10. Amene anaonongeka ku Endoro;Anakhala ngati ndowe ya kumunda.

11. Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu;Mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna:

12. Amene anati, TilandeMalo okhalamo Mulungu, akhale athu.

13. Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;Ngati ziputu zomka ndi mphepo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 83