Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 83:3-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Apangana mocenjerera pa anthu anu,Nakhalira upo pa obisika anu.

4. Amati, Tiyeni tiwaononge asakhalenso mtundu wa anthu;Ndipo dzina la Israyeli lisakumbukikenso.

5. Pakuti anakhalira upo ndi mtima umodzi;Anacita cipangano ca pa Inu:

6. Mahema a Edomu ndi a Aismayeli;Moabu ndi Ahagara;

7. Gebala ndi Amoni ndi Amaleki;Filistiya, pamodzi ndi iwo okhala m'Turo.

8. Asuri anaphatikana nao;Anakhala dzanja la ana a Loti,

9. Muwacitire monga munacitira Midyani;Ndi Sisera, ndi Jabini ku mtsinje wa Kisoni:

10. Amene anaonongeka ku Endoro;Anakhala ngati ndowe ya kumunda.

11. Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu;Mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna:

12. Amene anati, TilandeMalo okhalamo Mulungu, akhale athu.

13. Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;Ngati ziputu zomka ndi mphepo.

14. Monga moto upsereza nkhalango,Ndi monga lawi liyatsa mapiri;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 83