Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 83:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;Ngati ziputu zomka ndi mphepo.

14. Monga moto upsereza nkhalango,Ndi monga lawi liyatsa mapiri;

15. Momwemo muwatsate ndi namondwe,Nimuwaopse ndi kabvumvulu wanu.

16. Acititseni manyazi pankhope pao;Kuti afune dzina lanu, Yehova.

17. Acite manyazi, naopsedwe kosatha;Ndipo asokonezeke, naonongeke:

18. Kuti adziwe kuti inu nokha, dzina lanu ndinu Yehova,Ndinu Wam'mwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 83