Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 8:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. M'kamwa mwa makanda ndi oyamwamunakhazikitsamphamvu,Cifukwa ca otsutsana ndi Inu,Kuti muwaletse mdani ndi wobwezera cilango.

3. Pakuona ine thambo la kumwamba lanu, nchito ya zala zanu,Mwezi ndi nyenyezi, zimene munazikhazika,

4. Munthu ndani kuti mumkumbukila?Ndi mwana wa munthu kuti muceza naye?

5. Pakuti munamcepsa pang'ono ndi Mulungu,Munambveka iye korona wa ulemerero ndi ulemu.

6. Munamcititsa ufumu pa nchito za manja anu;Mudagonjetsa zonse pansi pa mapazi ace;

7. Nkhosa ndi ng'ombe, zonsezo,Ndi nyama za kuthengo zomwe;

8. Mbalame za m'mlengalenga, ndi nsomba za m'nyanja.Zopita m'njira za m'nyanja.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 8