Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 76:6-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo,Gareta ndi kavalo yemwe anagwa m'tulo.

7. Inu ndinu woopsa;Ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala ciriri ndani pamaso panu?

8. Mudamveketsa ciweruzo cocokera Kumwamba;Dziko lapansi linacita mantha, nilinakhala cete,

9. Pakuuka Mulungu kuti aweruze,Kuti apulumutse ofatsa onse a pa dziko lapansi.

10. Indedi, kuzaza kwace kwa munthu kudzakulemekezani;Cotsalira ca kuzazaku mudzaciletsa.

11. Windani ndipo citirani Yehova Mulungu wanu zowindazo;Onse akumzinga abwere naco copereka ca kwa Iye amene ayenera kumuopa.

12. Iye adzadula mzimu wa akulu;Akhala woopsa kwa mafumu a pa dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 76