Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 76:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mulungu adziwika mwa Yuda:Dzina lace limveka mwa Israyeli.

2. Msasa wace unali m'Salemu, Ndipo pokhala Iye m'Ziyoni.

3. Pomwepo anatyola mibvi ya paota;Cikopa, ndi lupanga, ndi nkhondo.

4. Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka wakuposa mapiri muli acifwamba.

5. Olimba mtima cifunkhidwa cuma cao, agona tulo tao;Amuna onse amphamvu asowa manja ao.

6. Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo,Gareta ndi kavalo yemwe anagwa m'tulo.

7. Inu ndinu woopsa;Ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala ciriri ndani pamaso panu?

Werengani mutu wathunthu Masalmo 76