Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 76:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mulungu adziwika mwa Yuda:Dzina lace limveka mwa Israyeli.

2. Msasa wace unali m'Salemu, Ndipo pokhala Iye m'Ziyoni.

3. Pomwepo anatyola mibvi ya paota;Cikopa, ndi lupanga, ndi nkhondo.

4. Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka wakuposa mapiri muli acifwamba.

5. Olimba mtima cifunkhidwa cuma cao, agona tulo tao;Amuna onse amphamvu asowa manja ao.

6. Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo,Gareta ndi kavalo yemwe anagwa m'tulo.

7. Inu ndinu woopsa;Ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala ciriri ndani pamaso panu?

8. Mudamveketsa ciweruzo cocokera Kumwamba;Dziko lapansi linacita mantha, nilinakhala cete,

9. Pakuuka Mulungu kuti aweruze,Kuti apulumutse ofatsa onse a pa dziko lapansi.

10. Indedi, kuzaza kwace kwa munthu kudzakulemekezani;Cotsalira ca kuzazaku mudzaciletsa.

11. Windani ndipo citirani Yehova Mulungu wanu zowindazo;Onse akumzinga abwere naco copereka ca kwa Iye amene ayenera kumuopa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 76