Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 72:4-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Adzaweruza ozunzika a mwa anthu,Adzapulumutsa ana aumphawi,Nadzaphwanya wosautsa.

5. Adzakuopani momwe likhalira dzuwa ndi mwezi,Kufikira mibadwo mibadwo.

6. Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga:Monga mvula yothirira dziko.

7. Masiku ace wolungama adzakhazikika;Ndi mtendere wocuruka, kufikira sipadzakhala mwezi.

8. Ndipo adzacita ufumu kucokera kunyanja kufikira kunyanja,Ndi kucokera ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko lapansi.

9. Okhala m'cipululu adzagwadira pamaso pace;Ndi adani ace adzaluma nthaka.

10. Mafumu a ku Tarisi ndi ku Zisumbuzo adzabwera naco copereka;Mafumu a ku Sheba ndi Seba adzadza nazo mphatso,

11. Inde mafumu onse adzamgwadira iye:Amitundu onse adzamtumikira.

12. Pakuti adzapulumutsa waumphawi wopfuulayo;Ndi wozunzika amene alibe mthandizi.

13. Adzacitira nsoni wosauka ndi waumphawi,Nadzapulumutsa moyo wa aumphawi,

14. Adzaombola moyo wao ku cinyengo ndi ciwawa;Ndipo mwazi wao udzakhala wa mtengo pamaso pace:

Werengani mutu wathunthu Masalmo 72