3. Mapiri adzatengera anthu mtendere,Timapiri tomwe, m'cilungamo.
4. Adzaweruza ozunzika a mwa anthu,Adzapulumutsa ana aumphawi,Nadzaphwanya wosautsa.
5. Adzakuopani momwe likhalira dzuwa ndi mwezi,Kufikira mibadwo mibadwo.
6. Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga:Monga mvula yothirira dziko.
7. Masiku ace wolungama adzakhazikika;Ndi mtendere wocuruka, kufikira sipadzakhala mwezi.
8. Ndipo adzacita ufumu kucokera kunyanja kufikira kunyanja,Ndi kucokera ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko lapansi.
9. Okhala m'cipululu adzagwadira pamaso pace;Ndi adani ace adzaluma nthaka.
10. Mafumu a ku Tarisi ndi ku Zisumbuzo adzabwera naco copereka;Mafumu a ku Sheba ndi Seba adzadza nazo mphatso,
11. Inde mafumu onse adzamgwadira iye:Amitundu onse adzamtumikira.
12. Pakuti adzapulumutsa waumphawi wopfuulayo;Ndi wozunzika amene alibe mthandizi.
13. Adzacitira nsoni wosauka ndi waumphawi,Nadzapulumutsa moyo wa aumphawi,
14. Adzaombola moyo wao ku cinyengo ndi ciwawa;Ndipo mwazi wao udzakhala wa mtengo pamaso pace: