Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 72:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Dzina lace lidzakhala kosatha:Momwe likhalira dzuwa dzina lace lidzamvekera zidzukulu:Ndipo anthu adzadalitsidwa mwa Iye;Amitundu onse adzamucha wodala.

18. Wolemekezeka Yehova Mulungu, Mulungu wa Israyeli,Amene acita zodabwiza yekhayo:

19. Ndipo dzina lace la ulemerero lidalitsike kosatha;Ndipo dziko lonse lapansi lidzale nao ulemerero wace.Amen, ndi Amen.

20. Mapemphero a Davide mwana wa Jese atha.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 72