Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 72:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Adzaombola moyo wao ku cinyengo ndi ciwawa;Ndipo mwazi wao udzakhala wa mtengo pamaso pace:

15. Ndipo iye adzakhala ndi moyo; ndipo adzampatsa golidi wa ku Sheba;Nadzampempherera kosalekeza;Adzamlemekeza tsiku lonse.

16. M'dzikomo mudzakhala dzinthu dzocuruka pamwamba pa mapiri;Zipatso zace zidzati waa, ngati za ku Lebano:Ndipo iwo a m'mudzi adzaphuka ngati msipu wapansi.

17. Dzina lace lidzakhala kosatha:Momwe likhalira dzuwa dzina lace lidzamvekera zidzukulu:Ndipo anthu adzadalitsidwa mwa Iye;Amitundu onse adzamucha wodala.

18. Wolemekezeka Yehova Mulungu, Mulungu wa Israyeli,Amene acita zodabwiza yekhayo:

Werengani mutu wathunthu Masalmo 72