Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 72:10-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Mafumu a ku Tarisi ndi ku Zisumbuzo adzabwera naco copereka;Mafumu a ku Sheba ndi Seba adzadza nazo mphatso,

11. Inde mafumu onse adzamgwadira iye:Amitundu onse adzamtumikira.

12. Pakuti adzapulumutsa waumphawi wopfuulayo;Ndi wozunzika amene alibe mthandizi.

13. Adzacitira nsoni wosauka ndi waumphawi,Nadzapulumutsa moyo wa aumphawi,

14. Adzaombola moyo wao ku cinyengo ndi ciwawa;Ndipo mwazi wao udzakhala wa mtengo pamaso pace:

15. Ndipo iye adzakhala ndi moyo; ndipo adzampatsa golidi wa ku Sheba;Nadzampempherera kosalekeza;Adzamlemekeza tsiku lonse.

16. M'dzikomo mudzakhala dzinthu dzocuruka pamwamba pa mapiri;Zipatso zace zidzati waa, ngati za ku Lebano:Ndipo iwo a m'mudzi adzaphuka ngati msipu wapansi.

17. Dzina lace lidzakhala kosatha:Momwe likhalira dzuwa dzina lace lidzamvekera zidzukulu:Ndipo anthu adzadalitsidwa mwa Iye;Amitundu onse adzamucha wodala.

18. Wolemekezeka Yehova Mulungu, Mulungu wa Israyeli,Amene acita zodabwiza yekhayo:

19. Ndipo dzina lace la ulemerero lidalitsike kosatha;Ndipo dziko lonse lapansi lidzale nao ulemerero wace.Amen, ndi Amen.

20. Mapemphero a Davide mwana wa Jese atha.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 72