Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 72:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Patsani mfumu maweruzo anu, Mulungu,Ndi mwana wa mfumu cilungamo canu.

2. Potero adzanenera anthu anu mlandu ndi m'cilungamo,Ndi ozunzika anu ndi m'ciweruzo.

3. Mapiri adzatengera anthu mtendere,Timapiri tomwe, m'cilungamo.

4. Adzaweruza ozunzika a mwa anthu,Adzapulumutsa ana aumphawi,Nadzaphwanya wosautsa.

5. Adzakuopani momwe likhalira dzuwa ndi mwezi,Kufikira mibadwo mibadwo.

6. Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga:Monga mvula yothirira dziko.

7. Masiku ace wolungama adzakhazikika;Ndi mtendere wocuruka, kufikira sipadzakhala mwezi.

8. Ndipo adzacita ufumu kucokera kunyanja kufikira kunyanja,Ndi kucokera ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko lapansi.

9. Okhala m'cipululu adzagwadira pamaso pace;Ndi adani ace adzaluma nthaka.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 72