Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 71:5-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pakuti Inu ndinu ciyembekezo canga, Ambuye Yehova;Mwandikhalira wokhulupirika kuyambira ubwana wanga.

6. Inu munandigwirizizakuyambira ndisanabadwe:Kuyambira pa thupi la mai wanga wondicitira zokoma ndinu;Ndidzakulemekezani kosalekeza.

7. Ndikhala codabwiza kwa ambiri;Koma Inu ndinu pothawira panga polimba.

8. M'kamwa mwanga mudzadzala lemekezo lanu,Ndi ulemu wanu tsiku lonse.

9. Musanditaye mu ukalamba wanga;Musandisiye, pakutha mphamvu yanga.

10. Pakuti adani anga alankhula za ine;Ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,

11. Ndi kuti, Wamsiya Mulungu:Mlondoleni, mgwireni; popeza palibe wompulumutsa,

12. Musandikhalire kutali, Mulungu;Fulumirani kundithandiza, Mulungu;

13. Adani a moyo wanga acite manyazi, nathawe;Cotonza ndi cimpepulo zikute ondifunira coipa,

14. Koma ine ndidzayembekeza kosaleka,Ndipo ndidzaonjeza kukulemekezani.

15. Pakamwa panga padzafotokozera cilungamo canu,Ndi cipulumutso canu tsiku lonse;Pakuti sindidziwa mawerengedwe ace.

16. Ndidzamuka mu mphamvu ya Ambuye Yehova;Ndidzachula cilungamo canu, inde canu cokha.

17. Mulungu, mwandiphunzitsa kuyambira ubwana wanga;Ndipo kufikira lero ndilalikira zodabwiza zanu.

18. Poteronso pokalamba ine ndi kukhala nazo imvi musandisiye, Mulungu;Kufikira nditalalikira mbadwo uwu za dzanja lanu,Mphamvu yanu kwa onse akudza m'mbuyo.

19. Cilungamo canunso, Mulungu, cifikira kuthambo;Inu amene munacita zazikuru,Akunga Inu ndani, Mulungu?

20. Inu, amene munationetsa nsautso zambiri ndi zoipa,Mudzatipatsanso moyo,Ndi kutitenganso munsi mwa dziko.

21. Mundionjezere ukulu wanga,Ndipo munditembenukire kundisangalatsa,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 71