Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 71:3-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mundikhalire thanthwe lokhalamo, lopitako kosaleka;Mwalamulira kundipulumutsa;Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

4. Ndilanditseni, Mulungu wanga, m'dzanja la woipa,M'dzanja la munthu wosalungama ndi waciwawa.

5. Pakuti Inu ndinu ciyembekezo canga, Ambuye Yehova;Mwandikhalira wokhulupirika kuyambira ubwana wanga.

6. Inu munandigwirizizakuyambira ndisanabadwe:Kuyambira pa thupi la mai wanga wondicitira zokoma ndinu;Ndidzakulemekezani kosalekeza.

7. Ndikhala codabwiza kwa ambiri;Koma Inu ndinu pothawira panga polimba.

8. M'kamwa mwanga mudzadzala lemekezo lanu,Ndi ulemu wanu tsiku lonse.

9. Musanditaye mu ukalamba wanga;Musandisiye, pakutha mphamvu yanga.

10. Pakuti adani anga alankhula za ine;Ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,

11. Ndi kuti, Wamsiya Mulungu:Mlondoleni, mgwireni; popeza palibe wompulumutsa,

12. Musandikhalire kutali, Mulungu;Fulumirani kundithandiza, Mulungu;

13. Adani a moyo wanga acite manyazi, nathawe;Cotonza ndi cimpepulo zikute ondifunira coipa,

14. Koma ine ndidzayembekeza kosaleka,Ndipo ndidzaonjeza kukulemekezani.

15. Pakamwa panga padzafotokozera cilungamo canu,Ndi cipulumutso canu tsiku lonse;Pakuti sindidziwa mawerengedwe ace.

16. Ndidzamuka mu mphamvu ya Ambuye Yehova;Ndidzachula cilungamo canu, inde canu cokha.

17. Mulungu, mwandiphunzitsa kuyambira ubwana wanga;Ndipo kufikira lero ndilalikira zodabwiza zanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 71