Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 71:17-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Mulungu, mwandiphunzitsa kuyambira ubwana wanga;Ndipo kufikira lero ndilalikira zodabwiza zanu.

18. Poteronso pokalamba ine ndi kukhala nazo imvi musandisiye, Mulungu;Kufikira nditalalikira mbadwo uwu za dzanja lanu,Mphamvu yanu kwa onse akudza m'mbuyo.

19. Cilungamo canunso, Mulungu, cifikira kuthambo;Inu amene munacita zazikuru,Akunga Inu ndani, Mulungu?

20. Inu, amene munationetsa nsautso zambiri ndi zoipa,Mudzatipatsanso moyo,Ndi kutitenganso munsi mwa dziko.

21. Mundionjezere ukulu wanga,Ndipo munditembenukire kundisangalatsa,

22. Ndiponso ndidzakuyamikani ndi cisakasa,Kubukitsa coonadi canu, Mulungu wanga;Ndidzakuyimbirani Nyimbo ndi zeze,Ndinu Woyerayo wa Israyeli.

23. Milomo yanga idzapfuula mokondwera poyimbira Inu Nyimbo;Inde, moyo wanga umene munaombola.

24. Lilime langa lomwe lidzalankhula za cilungamo canu tsiku lonse:Pakuti ofuna kundicitira coipa acita manyazi, nadodoma.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 71