Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 71:10-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Pakuti adani anga alankhula za ine;Ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,

11. Ndi kuti, Wamsiya Mulungu:Mlondoleni, mgwireni; popeza palibe wompulumutsa,

12. Musandikhalire kutali, Mulungu;Fulumirani kundithandiza, Mulungu;

13. Adani a moyo wanga acite manyazi, nathawe;Cotonza ndi cimpepulo zikute ondifunira coipa,

14. Koma ine ndidzayembekeza kosaleka,Ndipo ndidzaonjeza kukulemekezani.

15. Pakamwa panga padzafotokozera cilungamo canu,Ndi cipulumutso canu tsiku lonse;Pakuti sindidziwa mawerengedwe ace.

16. Ndidzamuka mu mphamvu ya Ambuye Yehova;Ndidzachula cilungamo canu, inde canu cokha.

17. Mulungu, mwandiphunzitsa kuyambira ubwana wanga;Ndipo kufikira lero ndilalikira zodabwiza zanu.

18. Poteronso pokalamba ine ndi kukhala nazo imvi musandisiye, Mulungu;Kufikira nditalalikira mbadwo uwu za dzanja lanu,Mphamvu yanu kwa onse akudza m'mbuyo.

19. Cilungamo canunso, Mulungu, cifikira kuthambo;Inu amene munacita zazikuru,Akunga Inu ndani, Mulungu?

Werengani mutu wathunthu Masalmo 71