Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 68:6-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Mulungu amangitsira banjaanthu a pa okha;Aturutsa am'ndende alemerere;Koma opikisana naye akhala m'dziko lopanda madzi.

7. Pakuturuka paja, Inu Mulungu, ndi kutsogolera anthu anu,Pakuyenda paja Inu m'cipululu;

8. Dziko lapansi linagwedezeka,Inde thambo linakhapamaso pa Mulungu;Sinai lomwe linagwedezeka pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israyeli.

9. Inu, Mulungu, munabvumbitsa cimvula,Munatsitsimutsa colowa canu pamene cidathodwa.

10. Gulu lanu linakhala m'dziko muja:Mwa ukoma wanu munalikonzera ozunzika, Mulungu.

11. Ambuye anapatsa mau:Akazi akulalikira uthengawo ndiwo khamu lalikuru.

12. Mafumu a magulu a ankhondo athawathawa:Ndipo mkazi amene akhala kwao agawa zofunkha.

13. Pogona inu m'makola a zoweta,Mukhala ngati mapiko a njiwa okulira ndi siliva,Ndi nthenga zace zokulira ndi golidi woyenga wonyezimira.

14. Pamene Wamphamvuyonse anabalalitsa mafumu m'dzikomo,Munayera ngati matalala m'Salimoni.

15. Phiri la Basana ndilo phiri la Mulungu;Phiri la Basana ndilo phiri la mitu mitu.

16. Mucitiranji nsanje mapiri inu a mitu mitu,Ndi phirilo Mulungu analikhumba, akhaleko?Inde, Yehova adzakhalabe komweko kosatha.

17. Magareta a Mulungu ndiwo zikwi makumi awiri, inde zikwi zowirikiza-wirikiza:Ambuye ali pakati pao, monga m'Sinai, m'malo opatulika,

18. Munakwera kumka kumwamba, munapita nao undende kuuyesa ndende;Munalandira zaufulu mwa anthu,Ngakhale mwa opikisana nanu, kuti Yehova Mulungu akakhale nao.

19. Wolemekezeka Ambuye, tsiku ndi tsiku atisenzera katundu,Ndiye Mulungu wa cipulumutso cathu.

20. Mulungu akhala kwa ife Mulungu wa cipulumutso;Ndipo Yehova Ambuye ali nazo zopulumutsira kuimfa.

21. Indedi Mulungu adzaphwanya mutu wa adani ace,Pakati pa mutu pa iye woyendabe m'kutsutsika kwace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 68