28. Mulungu wako analamulira mphamvu yako:Limbitsani, Mulungu, cimene munaticitira.
29. Cifukwa ca Kacisi wanu wa m'YerusalemuMafumu adzabwera naco caufulu kukupatsani.
30. Dzudzulani cirombo ca m'bango,Khamu la mphongo ndi zipfulula za anthu,Yense wakudzigonjera ndi ndarama zasiliva;Anabalalitsa mitundu ya anthu ya kukondwera nayo nkhondo.
31. Akulu adzafumira ku Aigupto;Kushi adzafulumira kutambalitsa manja ace kwa Mulungu.
32. Yimbirani Mulungu, maufumu a dziko lapansi inu;Yimbirani Ambuye zomlemekeza;
33. Kwa Iye wakuberekeka pamwambamwamba, oyambira kale lomwe;Taonani; amveketsa liu lace, ndilo liu lamphamvu.
34. Bvomerezani kuti mphamvu nja Mulungu;Ukulu wace uli pa Israyeli,Ndi mphamvu yace m'mitambo.
35. Inu Mulungu, ndinu woopsa m'malo oyera anu;Mulungu wa Israyeli ndiye amene apatsa anthu ace mphamvu ndi cilimbiko.Alemekezeke Mulungu.