Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 68:21-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Indedi Mulungu adzaphwanya mutu wa adani ace,Pakati pa mutu pa iye woyendabe m'kutsutsika kwace.

22. Ambuye anati, Ndidzawatenganso ku Basana,Ndidzawatenganso kozama kwa nyanja:

23. Kuti ubviike phazi lako m'mwazi,Kuti malilime a agaru ako alaweko adani ako.

24. Anapenya mayendedwe anu, Mulungu,Mayendedwe a Mulungu wanga, Mfumu yanga, m'malo oyera.

25. Oyimbira anatsogolera, oyimba zoyimba anatsata m'mbuyo,Pakatipo anamwali oyimba mangaka.

26. Lemekezani Mulungu m'masonkhano,Ndiye Ambuye, inu a gwero la Israyeli.

27. Apo pali Benjamini wamng'ono, wakuwacita ufumu,Akuru a Yuda, ndi a upo wao,Akulu a Zebuloni, akulu a Naftali.

28. Mulungu wako analamulira mphamvu yako:Limbitsani, Mulungu, cimene munaticitira.

29. Cifukwa ca Kacisi wanu wa m'YerusalemuMafumu adzabwera naco caufulu kukupatsani.

30. Dzudzulani cirombo ca m'bango,Khamu la mphongo ndi zipfulula za anthu,Yense wakudzigonjera ndi ndarama zasiliva;Anabalalitsa mitundu ya anthu ya kukondwera nayo nkhondo.

31. Akulu adzafumira ku Aigupto;Kushi adzafulumira kutambalitsa manja ace kwa Mulungu.

32. Yimbirani Mulungu, maufumu a dziko lapansi inu;Yimbirani Ambuye zomlemekeza;

33. Kwa Iye wakuberekeka pamwambamwamba, oyambira kale lomwe;Taonani; amveketsa liu lace, ndilo liu lamphamvu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 68