Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 68:19-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Wolemekezeka Ambuye, tsiku ndi tsiku atisenzera katundu,Ndiye Mulungu wa cipulumutso cathu.

20. Mulungu akhala kwa ife Mulungu wa cipulumutso;Ndipo Yehova Ambuye ali nazo zopulumutsira kuimfa.

21. Indedi Mulungu adzaphwanya mutu wa adani ace,Pakati pa mutu pa iye woyendabe m'kutsutsika kwace.

22. Ambuye anati, Ndidzawatenganso ku Basana,Ndidzawatenganso kozama kwa nyanja:

23. Kuti ubviike phazi lako m'mwazi,Kuti malilime a agaru ako alaweko adani ako.

24. Anapenya mayendedwe anu, Mulungu,Mayendedwe a Mulungu wanga, Mfumu yanga, m'malo oyera.

25. Oyimbira anatsogolera, oyimba zoyimba anatsata m'mbuyo,Pakatipo anamwali oyimba mangaka.

26. Lemekezani Mulungu m'masonkhano,Ndiye Ambuye, inu a gwero la Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 68