Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 68:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Auke Mulungu, abalalike adani ace;Iwonso akumuda athawe pamaso pace.

2. Muwacotse monga utsi ucotseka; Monga phula lisungunuka pamoto,Aonongeke oipa pamaso pa Mulungu.

3. Koma olungama akondwere; atumphe ndi cimwemwe pamaso pa Mulungu;Ndipo asekere naco cikondwerero.

4. Yimbirani Yehova, liyimbireni Nyimbo dzina lace;Undirani mseu Iye woberekekayo kucidikha;Dzina lace ndiye Yehova; ndipo tumphani ndi cimwemwe pamaso pace.

5. Mulungu, mokhala mwace mayera,Ndiye Atate wa ana amasiye, ndi woweruza wa akazi amasiye.

6. Mulungu amangitsira banjaanthu a pa okha;Aturutsa am'ndende alemerere;Koma opikisana naye akhala m'dziko lopanda madzi.

7. Pakuturuka paja, Inu Mulungu, ndi kutsogolera anthu anu,Pakuyenda paja Inu m'cipululu;

8. Dziko lapansi linagwedezeka,Inde thambo linakhapamaso pa Mulungu;Sinai lomwe linagwedezeka pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israyeli.

9. Inu, Mulungu, munabvumbitsa cimvula,Munatsitsimutsa colowa canu pamene cidathodwa.

10. Gulu lanu linakhala m'dziko muja:Mwa ukoma wanu munalikonzera ozunzika, Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 68