Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 66:9-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Iye amene asunga moyo wathu tingafe,Osalola phazi lathu literereke.

10. Pakati munatiyesera, Mulungu:Munatiyenga monga ayenga siliya.

11. Munapita nafe kuukonde;Munatisenza cothodwetsa pamsana pathu.

12. Munapititsa anthu oberekeka pamwamba pamitu pathu;Tinapyola moto ndi madzi; Koma munatifikitsa potitsitsimutsa.

13. Ndidzalowa m'nyumba yanu ndi nsembe zopsereza,Ndidzakucitirani zowinda zanga,

14. Zimene inazichula milomo yanga,Ndinazinena pakamwa panga pasautsika ine.

15. Ndidzakufukizirani nsembe zapsereza zonona,Pamodzi ndi cofukiza ca mphongo za nkhosa;Ndidzakonza ng'ombe pamodzi ndi mbuzi.

16. Idzani, imvani, inu nonse akuopa Mulungu,Ndipo ndidzafotokozera zonse anazicitira moyo wanga,

17. Ndinampfuulira Iye pakamwa panga,Ndipo ndinamkuza ndi lilime langa,

18. Ndikadasekera zopanda pace m'mtima mwanga,Ambuye sakadamvera:

19. Koma Mulungu anamvadi; Anamvera mau a pemphero langa,

20. Wolemekezeka Mulungu,Amene sanandipatutsira ine pemphero langa, kapena cifundo cace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 66