Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 62:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Moyo wanga ukhalira cete Mulungu yekha:Cipulumutso canga cifuma kwa Iye.

2. Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi cipulumutso canga;Msanje wanga, sindidzagwedezeka kwakukuru.

3. Mudzambvumbvulukira munthu mpaka liti,Kumupha iye, nonsenu,Monga khoma lopendekeka, ndi mpanda woweyeseka?

4. Komatu amkhaliraupo kuti amkankhire pansi ulemu wace;Akondwera nao mabodza;Adalitsa ndi m'kamwa mwao, Koma atemberera mumtima.

5. Moyo wanga, ukhalire cete Mulungu yekha;Pakuti ciyembekezo canga cifuma kwa Iye,

6. Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi cipulumutso canga,Msanje wanga, sindidzagwedezeka.

7. Pa Mulungu pali cipulumutso canga ndi ulemerero wanga:Thanthwe la mphamvu yanga ndi pothawirapo panga mpa Mulungu.

8. Khulupirani pa Iye nyengo zonse, anthu inu:Tsanulirani mitima yanu pamaso pace:Mulungu ndiye pothawirapo ife.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 62