Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 62:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Moyo wanga ukhalira cete Mulungu yekha:Cipulumutso canga cifuma kwa Iye.

2. Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi cipulumutso canga;Msanje wanga, sindidzagwedezeka kwakukuru.

3. Mudzambvumbvulukira munthu mpaka liti,Kumupha iye, nonsenu,Monga khoma lopendekeka, ndi mpanda woweyeseka?

4. Komatu amkhaliraupo kuti amkankhire pansi ulemu wace;Akondwera nao mabodza;Adalitsa ndi m'kamwa mwao, Koma atemberera mumtima.

5. Moyo wanga, ukhalire cete Mulungu yekha;Pakuti ciyembekezo canga cifuma kwa Iye,

6. Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi cipulumutso canga,Msanje wanga, sindidzagwedezeka.

7. Pa Mulungu pali cipulumutso canga ndi ulemerero wanga:Thanthwe la mphamvu yanga ndi pothawirapo panga mpa Mulungu.

8. Khulupirani pa Iye nyengo zonse, anthu inu:Tsanulirani mitima yanu pamaso pace:Mulungu ndiye pothawirapo ife.

9. Indetu, anthu acabe ndi mpweya, ndipo anthu akuru ndi bodza:Pakuwayesa apepuka;Onse pamodzi apepuka koposa mpweya,

10. Musakhulupirire kusautsa, ndipo musatama cifwamba;Cikacuruka cuma musakhazikepo mitima yanu.

11. Mulungu ananena kamodzi, ndinacimva kawiri:Kuti mphamvu ndi yace ya Mulungu:

12. Cifundonso ndi canu, Ambuye:Cifukwa Inu musudzula munthu ali yense monga mwa nchito yace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 62