Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 58:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Kodi muli cete ndithu poyenera inu kunena zolungama?Muweruza ana a anthu molunjika kodi?

2. Inde, mumtima mucita zosalungama;Pa dziko lapansi mugawira anthu ciwawa ca m'manja mwanu.

3. Oipa acita cilendo cibadwire:Asokera kuyambira kubadwa kwao, nanena bodza.

4. Ululu wao ukunga wa njoka;Akunga mphiri yogontha m'khutu, itseka m'khutu mwace.

5. Imene simvera liu la oitana,Akucita matsenga mocenieratu,

6. Tyolani mano ao m'kamwa mwao, Mulungu:Zulani zitsakano za misona ya mkango, Yehova.

7. Apitetu ngati madzi oyenda;Popiringidza mibvi yace ikhale yodukaduka.

8. Apite ngati nkhono yosungunuka;Asaone dzuwa monga mtayo,

9. Miphika yanu isanagwire moto waminga,Adzaiuluza, yaiwisi ndi yoyaka.

10. Wolungama adzakondwera pakuona kubwezera cilango:Adzasamba mapazi ace m'mwazi wa woipa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 58