Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 55:4-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Mtima wanga uwawa m'kati mwanga;Ndipo zoopsa za imfa zandigwera.

5. Mantha ndi kunjenjemera zandidzera,Ndipo zoopsetsa zandikuta.

6. Ndipo ndinati, Ha, wina akadandipatsa mapiko onga a njiwaMwenzi nditauluka, ndi kukhaliratu.

7. Onani, ndikadathawira kutari,Ndikadagona m'cipululu.

8. Ndikadafulumira ndipulumukeKu mphepo yolimba ndi namondwe.

9. Aonongeni, Ambuye, gawani lilime lao:Pakuti ndaona ciwawa ndi ndeu m'mudzimo.

10. Izizo ziuzungulira pa malinga ace usana ndi usiku;Ndipo m'kati mwace muli zapanda pace ndi cobvuta.

11. M'kati mwace muli kusakaza:Ciwawa ndi cinyengo sizicoka m'makwalala ace.

12. Pakuti si mdani amene ananditonzayo;Pakadatero ndikadacilola:Amene anadzikuza pa ine sindiye munthu wondida;Pakadatero ndikadambisalira:

13. Koma ameneyo ndiwe, munthu woyenerana nane,Tsamwali wanga, wodziwana nane.

14. Tinapangirana upo wokoma,Tinaperekeza khamu la anthu popita ku nyumba ya Mulungu.

15. Imfa iwagwere modzidzimutsa,Atsikire kumanda ali amoyo:Pakuti m'mokhala mwao muli zoipa pakati pao,

16. Koma ine ndidzapfuulira kwa Mulungu;Ndipo Yehova atizandipulumutsa.

17. Madzulo, m'mawa, ndi msana ndidzadandaula, ndi kubuula,Ndipo adzamva mau anga.

18. Anaombola moyo wanga ku nkhondo yondilaka, ndikhale mumtendere:Pakuti ndiwo ambiri okangana nane.

19. Mulungu adzamva, nadzawasautsa,Ndiye wokhalabe ciyambire kale lomwe.Popeza iwowa sasinthika konse,Ndipo saopa Mulungu.

20. Anaturutsa manja ace awagwire iwo akuyanjana naye:Anaipsa pangano lace.

21. Pakamwa pace mposalala ngati mafuta amkaka,Koma mumtima mwace munali nkhondo:Mau ace ngofewa ngati mafuta oyenga,Koma anali malupanga osololasolola.

22. Umsenze Yehova nkhawa zako, ndipo Iyeadzakugwiriziza:Nthawi zonse sadzalola wolungama agwedezeke.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 55