Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 52:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Potero Mulungu adzakupasula ku nthawi zonse,Adzakucotsa nadzakukwatula m'hema mwako,Nadzakuzula, kukucotsa m'dziko la amoyo.

6. Ndipo olungama adzaciona, nadzaopa,Nadzamseka, ndi kuti,

7. Tapenyani, suyu munthuyu amene sanamuyesa Mulungu mphamvu yace;Amene anatama kucuruka kwa cuma cace,Nadzilimbitsa m'kuipsa kwace.

8. Koma ine ndine ngati mtengo wauwisi waazitona m'nyumba ya Mulungu:Ndikhulupirira cifundo ca Mulungu ku nthawi za nthawi.

9. Ndidzakuyamikani kosatha, popeza Inu munacicita ici:Ndipo ndidzayembekeza dzina lanu, pakuti ici ncokoma, pamaso pa okondedwa anu,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 52