Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 50:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Adzafika Mulungu wathu, ndipo sadzakhala cete:Moto udzanyeka pankhope pace,Ndipo pozungulira pace padzasokosera kwakukuru.

4. Kumwamba adzaitana zakumwamba,Ndi dziko lapansi, kuti aweruze anthu ace:

5. Mundisonkhanitsire okondedwa anga;Amene anapangana ndi Ine ndi nsembe.

6. Ndipo zakumwamba zionetsera cilungamo cace;Pakuti Mulungu mwini wace ndiye woweruza.

7. Imvani, anthu anga, ndipo ndidzanena;Israyeli, ndipo ndidzacita mboni pa iwe:Ine Mulungu, ndine Mulungu wako.

8. Sindikudzudzula iwe cifukwa ca nsembe zako;Popeza nsembe zako zopsereza ziri pamaso panga cikhalire.

9. Sindidzatenga ng'ombe m'nyumbamwako,Kapena mbuzi m'makola mwako.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 50