Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 50:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Pakuona mbala, ubvomerezana nayo,Nucita nao acigololo.

19. Pakamwa pako mpocita zocimwa,Ndipo lilime lako likonza cinyengo.

20. Ukhala, nuneneza mbale wako;Usinjirira mwana wa mai wako.

21. Izi unazicita iwe, ndipo ndinakhala cete Ine;Unayesa kuti ndifanana nawe:Ndidzakudzudzula, ndi kucilongosola pamaso pako.

22. Dziwitsani ici inu oiwala Mulungu,Kuti ndingakumwetuleni, ndipo mungasowepo mpulumutsi:

23. Wopereka nsembe yaciyamiko andilemekeza Ine;Ndipo kwa iye wosunga mayendedwe aceNdidzamuonetsa cipulumutso ca Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 50