Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 50:17-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Popeza udana naco cilangizo,Nufulatira mau anga.

18. Pakuona mbala, ubvomerezana nayo,Nucita nao acigololo.

19. Pakamwa pako mpocita zocimwa,Ndipo lilime lako likonza cinyengo.

20. Ukhala, nuneneza mbale wako;Usinjirira mwana wa mai wako.

21. Izi unazicita iwe, ndipo ndinakhala cete Ine;Unayesa kuti ndifanana nawe:Ndidzakudzudzula, ndi kucilongosola pamaso pako.

22. Dziwitsani ici inu oiwala Mulungu,Kuti ndingakumwetuleni, ndipo mungasowepo mpulumutsi:

23. Wopereka nsembe yaciyamiko andilemekeza Ine;Ndipo kwa iye wosunga mayendedwe aceNdidzamuonetsa cipulumutso ca Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 50