13. Kodi ndidzadya nyama ya ng'ombe,Kapena kumwa mwazi wa mbuzi?
14. Pereka kwa Mulungu nsembe yaciyamiko;Numcitire Wam'mwambamwamba cowinda cako:
15. Ndipo undiitane tsiku la cisautso:Ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.
16. Koma kwa woipa Mulungu anena,Uli nao ciani malemba anga kulalikira,Ndi kuchula pangano langa pakamwa pako?
17. Popeza udana naco cilangizo,Nufulatira mau anga.