Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 50:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Kodi ndidzadya nyama ya ng'ombe,Kapena kumwa mwazi wa mbuzi?

14. Pereka kwa Mulungu nsembe yaciyamiko;Numcitire Wam'mwambamwamba cowinda cako:

15. Ndipo undiitane tsiku la cisautso:Ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.

16. Koma kwa woipa Mulungu anena,Uli nao ciani malemba anga kulalikira,Ndi kuchula pangano langa pakamwa pako?

17. Popeza udana naco cilangizo,Nufulatira mau anga.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 50