Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 50:12-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndikamva njala, sindidzakuuza:Pakuti dziko lonse ndi langa, ndi kudzala kwace komwe.

13. Kodi ndidzadya nyama ya ng'ombe,Kapena kumwa mwazi wa mbuzi?

14. Pereka kwa Mulungu nsembe yaciyamiko;Numcitire Wam'mwambamwamba cowinda cako:

15. Ndipo undiitane tsiku la cisautso:Ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.

16. Koma kwa woipa Mulungu anena,Uli nao ciani malemba anga kulalikira,Ndi kuchula pangano langa pakamwa pako?

17. Popeza udana naco cilangizo,Nufulatira mau anga.

18. Pakuona mbala, ubvomerezana nayo,Nucita nao acigololo.

19. Pakamwa pako mpocita zocimwa,Ndipo lilime lako likonza cinyengo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 50