Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 50:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndidziwa mbalame zonse za m'mapiri:Ndipo nyama za kuthengo ziri ndi Ine.

12. Ndikamva njala, sindidzakuuza:Pakuti dziko lonse ndi langa, ndi kudzala kwace komwe.

13. Kodi ndidzadya nyama ya ng'ombe,Kapena kumwa mwazi wa mbuzi?

14. Pereka kwa Mulungu nsembe yaciyamiko;Numcitire Wam'mwambamwamba cowinda cako:

15. Ndipo undiitane tsiku la cisautso:Ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.

16. Koma kwa woipa Mulungu anena,Uli nao ciani malemba anga kulalikira,Ndi kuchula pangano langa pakamwa pako?

Werengani mutu wathunthu Masalmo 50