Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 50:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Pakuti zamoyo zonse za kuthengo ndi zanga,Ndi ng'ombe za pa mapiri zikwi.

11. Ndidziwa mbalame zonse za m'mapiri:Ndipo nyama za kuthengo ziri ndi Ine.

12. Ndikamva njala, sindidzakuuza:Pakuti dziko lonse ndi langa, ndi kudzala kwace komwe.

13. Kodi ndidzadya nyama ya ng'ombe,Kapena kumwa mwazi wa mbuzi?

14. Pereka kwa Mulungu nsembe yaciyamiko;Numcitire Wam'mwambamwamba cowinda cako:

Werengani mutu wathunthu Masalmo 50