1. Mulungu wa milungu, Yehova, wanena,Aitana dziko lapansi kuyambira kuturuka kwa dzuwa kufikira kulowa kwace.
2. Mulungu awalira m'Ziyoni, mokongola mwangwiro.
3. Adzafika Mulungu wathu, ndipo sadzakhala cete:Moto udzanyeka pankhope pace,Ndipo pozungulira pace padzasokosera kwakukuru.
4. Kumwamba adzaitana zakumwamba,Ndi dziko lapansi, kuti aweruze anthu ace:
5. Mundisonkhanitsire okondedwa anga;Amene anapangana ndi Ine ndi nsembe.
6. Ndipo zakumwamba zionetsera cilungamo cace;Pakuti Mulungu mwini wace ndiye woweruza.