Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 50:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mulungu wa milungu, Yehova, wanena,Aitana dziko lapansi kuyambira kuturuka kwa dzuwa kufikira kulowa kwace.

2. Mulungu awalira m'Ziyoni, mokongola mwangwiro.

3. Adzafika Mulungu wathu, ndipo sadzakhala cete:Moto udzanyeka pankhope pace,Ndipo pozungulira pace padzasokosera kwakukuru.

4. Kumwamba adzaitana zakumwamba,Ndi dziko lapansi, kuti aweruze anthu ace:

5. Mundisonkhanitsire okondedwa anga;Amene anapangana ndi Ine ndi nsembe.

6. Ndipo zakumwamba zionetsera cilungamo cace;Pakuti Mulungu mwini wace ndiye woweruza.

7. Imvani, anthu anga, ndipo ndidzanena;Israyeli, ndipo ndidzacita mboni pa iwe:Ine Mulungu, ndine Mulungu wako.

8. Sindikudzudzula iwe cifukwa ca nsembe zako;Popeza nsembe zako zopsereza ziri pamaso panga cikhalire.

9. Sindidzatenga ng'ombe m'nyumbamwako,Kapena mbuzi m'makola mwako.

10. Pakuti zamoyo zonse za kuthengo ndi zanga,Ndi ng'ombe za pa mapiri zikwi.

11. Ndidziwa mbalame zonse za m'mapiri:Ndipo nyama za kuthengo ziri ndi Ine.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 50