Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 49:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndidzaoperanji masiku oipa,Pondizinga amphulupulu onditsata kucidendene?

6. Iwo akutama kulemera kwao;Nadzitamandira pa kucuruka kwa cuma cao;

7. Kuombola mbale sangadzamuombole,Kapena kumperekera dipo kwa Mulungu:

8. (Popeza ciombolo ca moyo wao nca mtengo wace wapatali,Ndipo cilekeke nthawi zonse)

9. Kuti akhale ndi moyo osafa,Osaona cibvundi.

10. Pakuti aona anzeru amafa,Monga aonongekera wopusa, wodyerera momwemo,Nasiyira ena cuma cao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 49