Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 49:2-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Awamba ndi omveka omwe,Acuma ndi aumphawi omwe.

3. Pakamwa panga padzanena zanzeru;Ndipo cilingiriro ca mtima wanga cidzakhala ca cidziwitso.

4. Ndidzachera khutu kufanizo:Ndidzafotokozera cophiphiritsa canga poyimbira.

5. Ndidzaoperanji masiku oipa,Pondizinga amphulupulu onditsata kucidendene?

6. Iwo akutama kulemera kwao;Nadzitamandira pa kucuruka kwa cuma cao;

7. Kuombola mbale sangadzamuombole,Kapena kumperekera dipo kwa Mulungu:

8. (Popeza ciombolo ca moyo wao nca mtengo wace wapatali,Ndipo cilekeke nthawi zonse)

9. Kuti akhale ndi moyo osafa,Osaona cibvundi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 49