12. Koma munthu wa ulemu wace sakhalitsa:Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.
13. Njira yao yino ndiyo kupusa kwao:Koma akudza m'mbuyo abvomereza mau ao.
14. Aikidwa m'manda ngati nkhosa;Mbusa wao ndi imfa:Ndipo m'mawa mwace oongoka mtima adzakhala mafumu ao;Ndipo maonekedwe ao adzanyekera kumanda, kuti pokhala pace padzasowa.
15. Koma Mulungu adzaombola moyo wanga ku mphamvu ya manda:Pakuti adzandilandira ine.
16. Usaope polemezedwa munthu,Pocuruka ulemu wa nyumba yace;
17. Pakuti pomwalira iye sadzamuka nako kanthu kali konse;Ulemu wace sutsika naye kumtsata m'mbuyo.
18. Angakhale anadalitsa moyo wace pokhala ndi moyo,Ndipo anthu akulemekeza iwe, podzicitira wekha zokoma,
19. Adzamuka ku mbadwo wa makolo ace;Sadzaona kuunika nthawi zonse.
20. Munthu waulemu, koma wosadziwitsa,Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.