Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 49:11-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Mumtima mwao ayesa kuti nyumba zao zikhala cikhalire,Ndi mokhala iwo ku mibadwo mibadwo;Achapo dzina lao padziko pao.

12. Koma munthu wa ulemu wace sakhalitsa:Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.

13. Njira yao yino ndiyo kupusa kwao:Koma akudza m'mbuyo abvomereza mau ao.

14. Aikidwa m'manda ngati nkhosa;Mbusa wao ndi imfa:Ndipo m'mawa mwace oongoka mtima adzakhala mafumu ao;Ndipo maonekedwe ao adzanyekera kumanda, kuti pokhala pace padzasowa.

15. Koma Mulungu adzaombola moyo wanga ku mphamvu ya manda:Pakuti adzandilandira ine.

16. Usaope polemezedwa munthu,Pocuruka ulemu wa nyumba yace;

17. Pakuti pomwalira iye sadzamuka nako kanthu kali konse;Ulemu wace sutsika naye kumtsata m'mbuyo.

18. Angakhale anadalitsa moyo wace pokhala ndi moyo,Ndipo anthu akulemekeza iwe, podzicitira wekha zokoma,

19. Adzamuka ku mbadwo wa makolo ace;Sadzaona kuunika nthawi zonse.

20. Munthu waulemu, koma wosadziwitsa,Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 49