Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 49:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Pakuti aona anzeru amafa,Monga aonongekera wopusa, wodyerera momwemo,Nasiyira ena cuma cao.

11. Mumtima mwao ayesa kuti nyumba zao zikhala cikhalire,Ndi mokhala iwo ku mibadwo mibadwo;Achapo dzina lao padziko pao.

12. Koma munthu wa ulemu wace sakhalitsa:Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.

13. Njira yao yino ndiyo kupusa kwao:Koma akudza m'mbuyo abvomereza mau ao.

14. Aikidwa m'manda ngati nkhosa;Mbusa wao ndi imfa:Ndipo m'mawa mwace oongoka mtima adzakhala mafumu ao;Ndipo maonekedwe ao adzanyekera kumanda, kuti pokhala pace padzasowa.

15. Koma Mulungu adzaombola moyo wanga ku mphamvu ya manda:Pakuti adzandilandira ine.

16. Usaope polemezedwa munthu,Pocuruka ulemu wa nyumba yace;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 49