Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 49:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Dzamveni kuno, anthu inu nonse;Cherani khutu, inu nonse amakono,

2. Awamba ndi omveka omwe,Acuma ndi aumphawi omwe.

3. Pakamwa panga padzanena zanzeru;Ndipo cilingiriro ca mtima wanga cidzakhala ca cidziwitso.

4. Ndidzachera khutu kufanizo:Ndidzafotokozera cophiphiritsa canga poyimbira.

5. Ndidzaoperanji masiku oipa,Pondizinga amphulupulu onditsata kucidendene?

6. Iwo akutama kulemera kwao;Nadzitamandira pa kucuruka kwa cuma cao;

7. Kuombola mbale sangadzamuombole,Kapena kumperekera dipo kwa Mulungu:

Werengani mutu wathunthu Masalmo 49