Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 45:7-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Mukonda cilungamo, ndipo mudana naco coipa:Cifukwa cace Mulungu, ndiye Mulungu wanu, wadzoza inuNdi mafuta a cikondwerero kuposa anzanu.

8. Zobvala zanu zonse nza mure, ndi khonje, ndi kasya;M'zinyumba za mfumu zomanga ndi minyanga ya njobvu mwatoruka zoyimba za zingwe zokukondweretsani.

9. Mwa omveka anu muli ana akazi amafumu:Ku dzanja lamanja lanu aima mkazi wa mfumu wobvala golidi wa ku Ofiri.

10. Tamvera, mwana wamkaziwe, taona, tachera khutu lako;Uiwalenso mtundu wako ndi nyumba ya atate wako;

11. Potero mfumuyo adzakhumba kukoma kwako:Pakuti ndiye mbuye wako; ndipo iwe umgwadire iye.

12. Ndipo mwana wamkazi wa Turo adzafika nayo mphatso;Acuma a mwa anthu adzapempha kudziwika nanu.

13. Mwana wamkazi wa mfumu ngwa ulemerero wonse m'kati mwa nyumba:Zobvala zace nza made agolidi.

14. Adzamtsogolera kwa mfumu wabvala zamawanga-mawanga:Anamwali anzace omtsata adzafika nao kwa inu.

15. Adzawatsogolera ndi cimwemwe ndi kusekerera:Adzalowa m'nyumba ya mfumu.

16. M'malo mwa makolo ako mudzakhala ana ako,Udzawaika akhale mafumu m'dziko lonse lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 45