Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 45:4-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo pindulani, m'ukulu wanu yendani,Kaamba ka coonadi ndi cifatso ndi cilungamo:Ndipo dzanja lanu lidzakuphunzitsani zoopsa.

5. Mibvi yanu njakuthwa;Mitundu ya anthu igwa pansi pa Inu:Iwalasa mumtima adani a mfumu.

6. Mpando wacifumu wanu, Mulungu, ukhala nthawi zonse zamkamuyaya:Ndodo yacifumu ya ufumu wanu ndiyo ndodo yolunjika.

7. Mukonda cilungamo, ndipo mudana naco coipa:Cifukwa cace Mulungu, ndiye Mulungu wanu, wadzoza inuNdi mafuta a cikondwerero kuposa anzanu.

8. Zobvala zanu zonse nza mure, ndi khonje, ndi kasya;M'zinyumba za mfumu zomanga ndi minyanga ya njobvu mwatoruka zoyimba za zingwe zokukondweretsani.

9. Mwa omveka anu muli ana akazi amafumu:Ku dzanja lamanja lanu aima mkazi wa mfumu wobvala golidi wa ku Ofiri.

10. Tamvera, mwana wamkaziwe, taona, tachera khutu lako;Uiwalenso mtundu wako ndi nyumba ya atate wako;

11. Potero mfumuyo adzakhumba kukoma kwako:Pakuti ndiye mbuye wako; ndipo iwe umgwadire iye.

12. Ndipo mwana wamkazi wa Turo adzafika nayo mphatso;Acuma a mwa anthu adzapempha kudziwika nanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 45