Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 45:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Adzamtsogolera kwa mfumu wabvala zamawanga-mawanga:Anamwali anzace omtsata adzafika nao kwa inu.

15. Adzawatsogolera ndi cimwemwe ndi kusekerera:Adzalowa m'nyumba ya mfumu.

16. M'malo mwa makolo ako mudzakhala ana ako,Udzawaika akhale mafumu m'dziko lonse lapansi.

17. Ndidzawakumbutsa dzina lanu m'mibadwo mibadwo:Cifukwa cace mitundu ya anthu idzayamika Inu ku nthawi za nthawi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 45