Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 45:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mtima wanga usefukira naco cinthu cokoma:Ndinena zopeka ine za mfumu:Lilime langa ndilo peni yofulumiza kulemba.

2. Inu ndinu wokongola ndithu kuposa ana a anthu;Anakutsanulirani cisomo pa milomo yanu:Cifukwa cace Mulungu anakudalitsani kosatha.

3. Dzimangireni lupanga lanu m'cuuno mwanu, wamphamvu inu,Ndi ulemerero wanu ndi ukulu wanu.

4. Ndipo pindulani, m'ukulu wanu yendani,Kaamba ka coonadi ndi cifatso ndi cilungamo:Ndipo dzanja lanu lidzakuphunzitsani zoopsa.

5. Mibvi yanu njakuthwa;Mitundu ya anthu igwa pansi pa Inu:Iwalasa mumtima adani a mfumu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 45