Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 42:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Madzi akuya aitanizana ndi madzi akuya,Pa mkokomo wa matiti anu: Mafunde onse a nyondonyondo anandimiza ine.

8. Koma usana Yehova adzalamulira cifundo cace,Ndipo usiku Nyimbo yace idzakhala ndi ine.Inde pemphero la kwa Yehova wa moyowanga.

9. Ndidzati kwa Mulungu, thanthwe langa, mwandiiwala cifukwa ninji?Ndimayenderanji wakulira Cifukwa ca kundipsinja mdaniyo?

10. Adani anga andinyoza ndi kundityola mafupa anga;Pakunena ndine dzuwa lonse,Mulungu wako ali kuti?

11. Udziweramiranji moyo wanga iwe?Ndi kuzingwa m'kati mwanga?Yembekeza Mulungu: pakuti ndidzamlemekeza tsopanonso,Ndiye cipulumutso ca nkhope yanga ndi Mulungu wanga,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 42