Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 42:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Monga nswala ipuma wefuwefu kukhumba mitsinje;Motero moyo wanga upuma wefuwefu kukhumba Inu, Mulungu.

2. Moyo wanga uli ndi ludzu la kwa Mulungu, la kwa Mulungu wamoyo:Ndikadze liti kuoneka pamaso pa Mulungu?

3. Misozi yanga yakhalangati cakudya canga,Usana ndi usiku;Pakunena iwo kwa ine dzuwa lonse,Mulungu wako ali kuti?

4. Ndizikumbukila izi ndipo nditsanulira moyo wanga m'kati mwa ine,Pakuti ndidafopita ndi unyinji wa anthu,Ndinawatsogolera ku nyumba ya Mulungu, ndi mau akuyimbitsa ndi kuyamika,Ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 42